Salimo 103:1-22

  • “Moyo wanga utamande Yehova”

    • Mulungu amatiikira kutali machimo athu (12)

    • Mulungu amasonyeza chifundo ngati bambo (13)

    • Mulungu amakumbukira kuti ndife fumbi (14)

    • Mpando wachifumu wa Yehova komanso ufumu wake (19)

    • Angelo amachita zimene Mulungu wanena (20)

Salimo la Davide. 103  Moyo wanga utamande Yehova.Chilichonse cha mkati mwanga, chitamande dzina lake loyera.   Moyo wanga utamande Yehova,Ndisaiwale zinthu zonse zimene wachita.+   Iye amakukhululukira zolakwa zako zonse+Ndipo amachiritsa matenda ako onse.+   Iye amawombola moyo wako kudzenje,*+Ndipo amakuveka chikondi chake chokhulupirika komanso chifundo ngati chisoti chachifumu.+   Iye amakupatsa zinthu zabwino+ nthawi yonse ya moyo wako, zimene umakhutira nazo,Kuti ukhalebe wachinyamata ndi wamphamvu ngati chiwombankhanga.+   Yehova amachita chilungamo+ kwa anthu onse oponderezedwaNdipo amaweruza milandu yawo mwachilungamo.+   Anadziwitsa Mose njira zake,+Ndipo ana a Isiraeli anawadziwitsa zochita zake.+   Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima,*+Wosakwiya msanga ndiponso wachikondi chokhulupirika chochuluka.*+   Iye sadzakhalira kutipezera zifukwa nthawi zonse,+Kapena kutisungira mkwiyo mpaka kalekale.+ 10  Sanatichitire mogwirizana ndi machimo athu,+Kapena kutipatsa chilango chogwirizana ndi zolakwa zathu.+ 11  Mofanana ndi mmene kumwamba kulili pamwamba kwambiri kuposa dziko lapansi,Chikondi chokhulupirika chimene amasonyeza anthu amene amamuopa ndi chachikulu kwambiri.+ 12  Mofanana ndi mmene kotulukira dzuwa kwatalikirana ndi kolowera dzuwa,Mulungu waikanso zolakwa zathu kutali ndi ife.+ 13  Mofanana ndi bambo amene amasonyeza chifundo kwa ana ake,Yehova wasonyezanso chifundo kwa anthu amene amamuopa.+ 14  Chifukwa iye akudziwa bwino mmene anatipangira,+Amakumbukira kuti ndife fumbi.+ 15  Masiku a moyo wa munthu ali ngati masiku a udzu.+Iye amaphuka ngati duwa lakutchire.+ 16  Koma mphepo ikawomba limafa,Ndipo zimangokhala ngati panalibepo.* 17  Koma Yehova adzapitiriza kusonyeza chikondi chake chokhulupirika mpaka kalekaleKwa anthu amene amamuopa,+Ndipo adzapitiriza kusonyeza chilungamo chake kwa ana a ana awo.+ 18  Adzapitiriza kuchita zimenezi kwa anthu amene amasunga pangano lake,+Ndi kwa anthu amene amatsatira malamulo ake mosamala. 19  Yehova wakhazikitsa mpando wake wachifumu kumwamba.+Ndipo ufumu wake ukulamulira chilichonse.+ 20  Tamandani Yehova, inu angelo ake onse+ amphamvu,Amene amamvera mawu ake komanso kuchita zimene wanena.+ 21  Tamandani Yehova, inu magulu ake onse a angelo,+Atumiki ake amene amachita chifuniro chake.+ 22  Tamandani Yehova, inu ntchito zake zonse,Mʼmalo onse amene iye akulamulira. Moyo wanga wonse utamande Yehova.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “kumanda.”
Kapena kuti, “ndi wachisomo.”
Kapena kuti, “ndiponso wosonyeza kukoma mtima kosatha.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndipo pamalo amene linali salidziwanso.”