Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

FUNSO 13

Kodi Baibulo Limati Chiyani pa Nkhani ya Ntchito?

“Kodi wamuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzaima pamaso pa mafumu. Sadzaima pamaso pa anthu wamba.”

Miyambo 22:29

“Munthu wakuba asiye kubako, koma azigwira ntchito molimbikira. Azigwira ntchito yabwino ndi manja ake kuti azitha kupeza zinthu zimene angathe kugawana ndi munthu wosowa.”

Aefeso 4:28

“Munthu aliyense adye ndi kumwa nʼkumasangalala ndi zinthu zabwino, chifukwa cha ntchito yake yonse imene waigwira mwakhama. Imeneyi ndi mphatso yochokera kwa Mulungu.”

Mlaliki 3:13