Wolembedwa ndi Mateyu 24:1-51

  • CHIZINDIKIRO CHA KUKHALAPO KWA KHRISTU (1-51)

    • Nkhondo, njala, zivomerezi (7)

    • Uthenga wabwino udzalalikidwa (14)

    • Chisautso chachikulu (21, 22)

    • Chizindikiro cha Mwana wa munthu (30)

    • Mtengo wa mkuyu (32-34)

    • Mofanana ndi masiku a Nowa (37-39)

    • Khalanibe maso (42-44)

    • Kapolo wokhulupirika komanso kapolo woipa (45-51)

24  Pamene Yesu ankachoka kukachisi, ophunzira ake anabwera kwa iye kuti amuonetse nyumba zapakachisipo.  Koma iye anawauza kuti: “Kodi simukuziona zinthu zonsezi? Ndithu ndikukuuzani, pano sipadzatsala mwala uliwonse pamwamba pa mwala unzake umene sudzagwetsedwa.”+  Atakhala pansi mʼphiri la Maolivi, ophunzira anabwera kwa iye ali payekha nʼkumufunsa kuti: “Tiuzeni, kodi zinthu zimenezi zidzachitika liti, ndipo chizindikiro cha kukhalapo* kwanu+ ndi cha mapeto a nthawi* ino+ chidzakhala chiyani?”  Poyankha Yesu ananena kuti: “Samalani kuti munthu asakusocheretseni,+  chifukwa ambiri adzabwera mʼdzina langa nʼkunena kuti, ‘Khristu uja ndine,’ ndipo adzasocheretsa anthu ambiri.+  Mudzamva phokoso la nkhondo ndi malipoti a nkhondo. Izitu zisadzakuchititseni mantha, chifukwa zimenezi zikuyenera kuchitika ndithu, koma mapeto adzakhala asanafikebe.+  Mtundu udzaukirana ndi mtundu wina ndipo ufumu udzaukirana ndi ufumu wina.+ Kudzakhala njala+ ndi zivomerezi mʼmalo osiyanasiyana.+  Zonsezi ndi chiyambi cha mavuto aakulu.*  Kenako anthu adzakuperekani kuti mukazunzidwe+ ndipo adzakuphani.+ Anthu a mitundu yonse adzadana nanu chifukwa cha dzina langa.+ 10  Pa nthawiyo anthu ambiri adzapunthwa ndipo adzaperekana komanso kudana. 11  Kudzakhala aneneri ambiri abodza ndipo adzasocheretsa anthu ambiri.+ 12  Chifukwa cha kuwonjezeka kwa kusamvera malamulo, chikondi cha anthu ambiri chidzazirala. 13  Koma amene adzapirire* mpaka pamapeto ndi amene adzapulumuke.+ 14  Uthenga wabwino uwu wa Ufumu udzalalikidwa padziko lonse lapansi kumene kuli anthu, kuti ukhale umboni kwa anthu amitundu yonse,+ kenako mapeto adzafika. 15  Choncho mukadzaona chinthu chonyansa chobweretsa chiwonongeko, chimene Mneneri Danieli ananena, chitaima mʼmalo oyera+ (wowerenga adzazindikire), 16  amene ali mu Yudeya adzayambe kuthawira kumapiri.+ 17  Munthu amene ali padenga la nyumba asadzatsike kukatenga katundu mʼnyumba mwake. 18  Munthu amene ali mʼmunda asadzabwerere kukatenga malaya ake akunja. 19  Tsoka kwa akazi oyembekezera komanso oyamwitsa ana mʼmasiku amenewo! 20  Pitirizani kupemphera kuti musadzathawe mʼnyengo ya chisanu kapena pa tsiku la Sabata. 21  Chifukwa pa nthawiyo kudzakhala chisautso chachikulu+ chimene sichinachitikepo kuchokera pachiyambi cha dziko mpaka lero, ndipo sichidzachitikanso.+ 22  Kunena zoona, masikuwo akanapanda kufupikitsidwa, palibe amene akanapulumuka. Koma chifukwa cha osankhidwawo, masikuwo adzafupikitsidwa.+ 23  Choncho munthu akadzakuuzani kuti, ‘Onani! Khristu uja ali kuno,’+ kapena, ‘Ali uko!’ musadzakhulupirire zimenezo.+ 24  Chifukwa kudzabwera anthu onamizira kuti ndi Khristu komanso aneneri abodza+ ndipo adzachita zizindikiro zamphamvu ndiponso zodabwitsa, kuti ngati nʼkotheka, adzasocheretse+ ngakhale osankhidwawo. 25  Onani! Ine ndakuchenjezani zimenezi zisanachitike. 26  Choncho anthu akadzakuuzani kuti, ‘Taonani! Ali mʼchipululu,’ musadzapiteko. Akadzati, ‘Taonani! Ali mʼzipinda zamkati,’ musadzakhulupirire zimenezo.+ 27  Chifukwa mofanana ndi mmene mphezi imangʼanimira kuchokera kumʼmawa nʼkuwala mpaka kukafika kumadzulo, zidzakhalanso choncho ndi kukhalapo* kwa Mwana wa munthu.+ 28  Kulikonse kumene kuli chinthu chakufa, ziwombankhanga zidzasonkhana komweko.+ 29  Chisautso cha masiku amenewo chikadzangotha, dzuwa lidzachita mdima+ ndipo mwezi sudzapereka kuwala kwake. Nyenyezi zidzagwa kuchokera kumwamba ndipo mphamvu zakumwamba zidzagwedezeka.+ 30  Kenako chizindikiro cha Mwana wa munthu chidzaonekera kumwamba ndipo mafuko onse apadziko lapansi adzadziguguda pachifuwa chifukwa cha chisoni.+ Iwo adzaona Mwana wa munthu+ akubwera pamitambo ya kumwamba ndi mphamvu ndiponso ulemerero waukulu.+ 31  Iye adzatumiza angelo ake ndi kulira kwamphamvu kwa lipenga ndipo adzasonkhanitsa osankhidwa ake kuchokera kumphepo 4, kuchokera kumalekezero amumlengalenga mpaka kumalekezero ena.+ 32  Tsopano phunzirani zokhudza mtengo wa mkuyu kuchokera pa fanizo ili: Nthambi yake yanthete ikaphuka nʼkuchita masamba, mumadziwa kuti chilimwe chili pafupi.+ 33  Chimodzimodzi inunso, mukadzaona zinthu zonsezi, mudzadziwe kuti iye ali pafupi, ali pakhomo penipeni.+ 34  Ndithu ndikukuuzani kuti mʼbadwo uwu sudzatha wonse kufa, mpaka zinthu zonsezi zitachitika. 35  Kumwamba ndi dziko lapansi zidzachoka, koma mawu anga adzakhalapo mpaka kalekale.+ 36  Kunena za tsiku limenelo ndi ola lake, palibe amene akudziwa,+ ngakhale angelo akumwamba kapenanso Mwana, kupatulapo Atate wokha.+ 37  Chifukwa mofanana ndi mmene masiku a Nowa analili,+ ndi mmenenso kukhalapo* kwa Mwana wa munthu kudzakhalire.+ 38  Mʼmasiku amenewo Chigumula chisanafike, anthu ankadya ndi kumwa. Amuna ankakwatira ndipo akazi ankakwatiwa mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchingalawa.+ 39  Anthu ananyalanyaza zimene zinkachitika mpaka Chigumula chinafika nʼkuwaseseratu onsewo.+ Zidzakhalanso choncho ndi kukhalapo kwa Mwana wa munthu. 40  Pa nthawiyo, amuna awiri adzakhala ali mʼmunda. Mmodzi adzatengedwa ndipo winayo adzasiyidwa. 41  Akazi awiri adzakhala akupera pamphero. Mmodzi adzatengedwa ndipo winayo adzasiyidwa.+ 42  Choncho khalanibe maso chifukwa simukudziwa tsiku limene Ambuye wanu adzabwere.+ 43  Koma dziwani izi: Ngati mwininyumba atadziwa nthawi imene wakuba angabwere,+ angakhale maso ndipo sangalole kuti wakubayo athyole nʼkulowa mʼnyumba mwake.+ 44  Pa chifukwa chimenechi, inunso khalani okonzeka,+ chifukwa Mwana wa munthu adzabwera pa ola limene simukuliganizira. 45  Kodi ndi ndani kwenikweni amene ndi kapolo wokhulupirika komanso wanzeru amene mbuye wake anamuika kuti aziyangʼanira antchito ake apakhomo, nʼkumawapatsa chakudya pa nthawi yoyenera?+ 46  Kapolo ameneyo adzakhala wosangalala, ngati mbuye wake pobwera adzamupeze akuchita zimenezo!+ 47  Ndithu ndikukuuzani, adzamuika kuti aziyangʼanira zinthu zake zonse. 48  Koma ngati kapolo ameneyu angasonyeze kuti ndi woipa nʼkuyamba kunena mumtima mwake kuti, ‘Mbuye wanga akuchedwa,’+ 49  nʼkuyamba kumenya akapolo anzake komanso kudya ndi kumwa limodzi ndi zidakwa zenizeni, 50  mbuye wa kapoloyo adzabwera pa tsiku limene iye sakuyembekezera ndi pa ola limene sakulidziwa.+ 51  Choncho adzamupatsa chilango choopsa ndipo adzamuponya kumene kuli anthu achinyengo. Kumeneko iye adzalira komanso kukukuta mano.”+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “chiyambi cha mavuto aakulu ngati ululu umene mzimayi amamva akatsala pangʼono kubereka.”
Kapena kuti, “amene wapirira.”