Wolembedwa ndi Mateyu 10:1-42

  • Atumwi 12 (1-4)

  • Malangizo okhudza kulalikira (5-15)

  • Ophunzira adzazunzidwa (16-25)

  • Muziopa Mulungu, osati anthu (26-31)

  • Osati mtendere, koma lupanga (32-39)

  • Kulandira ophunzira a Yesu (40-42)

10  Choncho anaitana ophunzira ake 12 nʼkuwapatsa mphamvu kuti azitha kutulutsa mizimu yoipa+ komanso kuchiritsa matenda a mtundu uliwonse amene anthu ankadwala.  Mayina a atumwi 12 ndi awa:+ Simoni, amene ankatchulidwa kuti Petulo*+ ndi Andireya+ mchimwene wake. Yakobo mwana wa Zebedayo ndi mchimwene wake Yohane.+  Filipo ndi Batolomeyo,+ Tomasi+ ndi Mateyu+ wokhometsa msonkho, Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Tadeyo.  Simoni Kananiya* ndi Yudasi Isikariyoti, amene pambuyo pake anapereka Yesu.+  Yesu anatumiza atumwi 12 amenewa ndipo anawapatsa malangizo awa:+ “Musapite mumsewu wa anthu a mitundu ina ndipo musalowe mumzinda uliwonse wa Asamariya.+  Mʼmalomwake, nthawi zonse muzipita kwa nkhosa zosochera za nyumba ya Isiraeli.+  Mukapita muzikalalikira kuti, ‘Ufumu wakumwamba wayandikira.’+  Muzichiritsa odwala,+ kuukitsa anthu akufa, kuyeretsa akhate komanso kutulutsa ziwanda. Munalandira kwaulere, muzipereka kwaulere.  Musatenge golide, siliva kapena kopa* mʼzikwama zanu za ndalama.+ 10  Musatenge thumba la chakudya cha pa ulendo kapena malaya awiri* kapena nsapato kapenanso ndodo+ chifukwa wantchito ayenera kulandira chakudya chake.+ 11  Mukalowa mumzinda kapena mʼmudzi uliwonse, muzifufuza yemwe ali woyenerera kumuuza uthenga wanu, ndipo muzikhala mʼnyumba yake mpaka nthawi yochoka.+ 12  Mukalowa mʼnyumba, muzipereka moni kwa anthu a mʼbanjamo. 13  Ngati akulandirani bwino, mtendere umene mukuwafunira ukhale pa anthuwo,+ koma ngati sanakulandireni bwino, mtendere wanu ubwerere kwa inu. 14  Kulikonse kumene munthu sakakulandirani kapena kumvetsera mawu anu, mukamatuluka mʼnyumba imeneyo kapena mumzinda umenewo muzisansa fumbi kumapazi anu.+ 15  Ndithu ndikukuuzani, chilango cha mzinda umenewo chidzakhala chopweteka kwambiri pa Tsiku la Chiweruzo kuposa cha Sodomu ndi Gomora.+ 16  Taonani! Ndikukutumizani ngati nkhosa pakati pa mimbulu. Choncho muzichita zinthu mochenjera ngati njoka koma moona mtima ngati nkhunda.+ 17  Chenjerani ndi anthu, chifukwa adzakutengerani kumakhoti aangʼono,+ ndipo adzakukwapulani+ mumasunagoge awo.+ 18  Adzakupititsani kwa abwanamkubwa ndi mafumu+ chifukwa ndinu otsatira anga, kuti iwowo komanso anthu a mitundu ina aphunzire za ine.+ 19  Koma akadzakupititsani kumeneko, musadzade nkhawa kuti mudzalankhula bwanji kapena kuti mudzanena chiyani, chifukwa zoti mulankhule mudzapatsidwa nthawi yomweyo.+ 20  Zili choncho chifukwa wolankhula simudzakhala inu nokha, koma mzimu wa Atate wanu udzalankhula kudzera mwa inu.+ 21  Komanso munthu adzapereka mʼbale wake kuti aphedwe ndipo bambo adzapereka mwana wake. Ana adzaukira makolo awo ndipo adzachititsa kuti aphedwe.+ 22  Anthu onse adzadana nanu chifukwa cha dzina langa,+ koma amene adzapirire* mpaka mapeto ndi amene adzapulumuke.+ 23  Akakuzunzani mumzinda umodzi, muthawire mumzinda wina.+ Ndithu ndikukuuzani, simudzamaliza kuzungulira mizinda yonse ya Isiraeli Mwana wa munthu asanafike. 24  Wophunzira saposa mphunzitsi wake ndipo kapolo saposa mbuye wake.+ 25  Wophunzira amangofanana ndi mphunzitsi wake ndipo kapolo amangofanana ndi mbuye wake.+ Ngati anthu atchula mwininyumba kuti Belezebule,*+ kuli bwanji ena a mʼbanja lakelo? 26  Choncho musawaope, chifukwa palibe chobisika chimene sichidzaululika ndipo palibe chinsinsi chimene sichidzadziwika.+ 27  Zimene ndimakuuzani mumdima, muzinene poyera, ndipo zimene mumamva anthu akunongʼonezana, muzilalikire muli padenga.+ 28  Musachite mantha ndi amene amapha thupi koma sangathe kupha moyo.+ Mʼmalomwake, muziopa amene angathe kuwononga zonse ziwiri, moyo ndi thupi lomwe mʼGehena.*+ 29  Mpheta ziwiri amazigulitsa kakhobidi kamodzi kochepa mphamvu,* si choncho? Koma palibe ngakhale imodzi imene idzagwa pansi Atate wanu osadziwa.+ 30  Ndipotu ngakhale tsitsi lonse lamʼmutu mwanu amaliwerenga. 31  Choncho musachite mantha, ndinu ofunika kwambiri kuposa mpheta zambiri.+ 32  Choncho aliyense amene akuvomereza pamaso pa anthu kuti ndi wophunzira wanga,+ inenso ndidzamuvomereza pamaso pa Atate wanga wakumwamba kuti ndi wophunzira wanga.+ 33  Koma aliyense amene adzandikane pamaso pa anthu, inenso ndidzamukana pamaso pa Atate wanga wakumwamba.+ 34  Musaganize kuti ndinabwera kudzabweretsa mtendere padziko lapansi. Sindinabwere kuti ndidzabweretse mtendere koma lupanga.+ 35  Ndinabwera kudzagawanitsa anthu. Ndinabwera kudzachititsa kuti mwana wamwamuna atsutsane ndi bambo ake, mwana wamkazi atsutsane ndi mayi ake ndiponso kuti mkazi wokwatiwa atsutsane ndi apongozi ake aakazi.+ 36  Kunena zoona, adani a munthu adzakhala a mʼbanja lake lenileni. 37  Aliyense amene amakonda kwambiri bambo ake kapena mayi ake kuposa ine ndi wosayenera kuti akhale wophunzira wanga. Komanso aliyense amene amakonda kwambiri mwana wake wamwamuna kapena wamkazi kuposa ine ndi wosayenera kuti akhale wophunzira wanga.+ 38  Ndiponso aliyense amene sakufuna kunyamula mtengo wake wozunzikirapo* nʼkupitiriza kunditsatira ndi wosayenera kuti akhale wophunzira wanga.+ 39  Aliyense amene akuyesa kupulumutsa moyo wake adzautaya, koma amene wataya moyo wake chifukwa cha ine adzaupeza.+ 40  Amene wakulandirani walandiranso ine ndipo amene walandira ine walandiranso amene anandituma.+ 41  Amene walandira mneneri chifukwa ndi mneneri adzalandira mphoto yofanana ndi imene mneneri amalandira,+ ndipo amene walandira munthu wolungama chifukwa ndi wolungama adzalandira mphoto yofanana ndi imene munthu wolungama amalandira. 42  Aliyense wopatsa mmodzi wa tiana iti ngakhale madzi ozizira okha mʼkapu kuti amwe chifukwa ndi wophunzira wanga, ndithu ndikukuuzani, ameneyo mphoto yake sidzatayika ngakhale pangʼono.”+

Mawu a M'munsi

“Petulo” amadziwika ndi mayina 5. Pano akutchulidwa kuti “Simoni, amene ankatchulidwa kuti Petulo.” Pa Mt 16:16 akutchulidwa kuti “Simoni Petulo,” pa Mac 15:14, “Sumiyoni,” ndipo pa Yoh 1:42, “Kefa.” Koma nthawi zambiri amatchulidwa kuti “Petulo,” monga mmene zilili pa Mt 14:28.
Kapena kuti, “wakhama.”
Kapena kuti, “mkuwa.”
Kapena kuti, “malaya owonjezera.”
Kapena kuti, “amene wapirira.”
Dzina limene Satana, yemwe ndi kalonga kapena kuti wolamulira ziwanda, amadziwika nalo.
Mʼchilankhulo choyambirira, “asariyoni imodzi,” Onani Zakumapeto B14.