Yeremiya 10:1-25

  • Milungu ya anthu a mitundu ina singafanane ndi Mulungu wamoyo (1-16)

  • Nthawi yoti awonongedwe komanso kutengedwa kupita kudziko lina yayandikira (17, 18)

  • Yeremiya anamva chisoni (19-22)

  • Pemphero la mneneri (23-25)

    • Munthu alibe ulamuliro wosankha yekha njira ya moyo wake (23)

10  Inu a mʼnyumba ya Isiraeli, imvani chenjezo limene Yehova wakupatsani.  Yehova wanena kuti: “Musaphunzire miyambo ya anthu a mitundu ina,+Ndipo musachite mantha ndi zizindikiro zakumwamba,Chifukwa anthu a mitundu ina amachita mantha ndi zizindikirozo.+   Miyambo ya anthu amenewa ndi yopanda pake. Mmisiri amagwetsa mtengo munkhalango,Nʼkusema fano pogwiritsa ntchito chida chake.*+   Akatero amakongoletsa fanolo ndi siliva komanso golide.+Kenako amatenga hamala ndi misomali nʼkulikhomerera pansi kuti lisagwe.+   Mafanowo ali ngati choopsezera mbalame mʼmunda wa minkhaka ndipo sangalankhule.+Iwo amafunika kunyamulidwa chifukwa sangayende okha.+ Musamachite mantha ndi mafano chifukwa sangakuvulazeni,Komanso sangachite chilichonse chabwino.”+   Palibe aliyense amene angafanane ndi inu Yehova.+ Inu ndinu wamkulu ndipo dzina lanu ndi lalikulu komanso lamphamvu.   Kodi ndi ndani amene sakuyenera kukuopani, inu Mfumu ya mitundu yonse?+ Inuyo ndinu woyenera kuopedwa.Chifukwa pakati pa anzeru onse a mʼmitundu ya anthu ndiponso pakati pa maufumu awo onse,Palibiretu aliyense wofanana ndi inu.+   Onse ndi opanda nzeru ndiponso opusa.+ Malangizo ochokera pamtengo amalimbikitsa anthu kuchita zachabechabe.+   Siliva amene anamusula kukhala mapalemapale amachokera ku Tarisi+ ndipo golide amachokera ku Ufazi.Zonsezi zimakonzedwa mwaluso ndipo ndi ntchito ya manja a mmisiri wa zitsulo. Amawaveka zovala zaulusi wabuluu ndi ubweya wa nkhosa wapepo. Mafano onsewo amapangidwa ndi amisiri aluso. 10  Koma Yehova ndi Mulungu woonadi. Iye ndi Mulungu wamoyo+ ndipo ndi Mfumu yamuyaya.+ Dziko lapansi lidzagwedezeka chifukwa cha mkwiyo wake,+Ndipo palibe mitundu ya anthu imene idzapilire mkwiyo wake. 11 * Mitunduyo ukaiuze izi: “Milungu imene sinapange kumwamba ndi dziko lapansiIdzawonongedwa padziko lapansi komanso pansi pa thambo.”+ 12  Iye ndi Mulungu amene anapanga dziko lapansi pogwiritsa ntchito mphamvu zake,Amene anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru zake.+Amenenso anatambasula kumwamba chifukwa cha kuzindikira kwake.+ 13  Mawu ake akamveka,Madzi akumwamba amachita mkokomo,+Ndipo amachititsa mitambo* kukwera kuchokera kumalekezero a dziko lapansi.+ Iye amachititsa kuti kukamagwa mvula mphezi zizingʼanima,Ndipo amatulutsa mphepo mʼnyumba zake zosungira.+ 14  Munthu aliyense akuchita zinthu mopanda nzeru komanso mosazindikira. Mmisiri wa zitsulo aliyense adzachita manyazi chifukwa cha chifaniziro chake chosula.+Chifukwa chifaniziro chake chopangidwa ndi chitsulo chosungunula ndi mulungu wonamaNdipo mafano amenewa alibe mzimu.*+ 15  Iwo ndi achabechabe, oyenera kunyozedwa.+ Tsiku loti aweruzidwe likadzafika adzawonongedwa. 16  Koma Mulungu, amene ndi cholowa cha Yakobo, sali ngati mafano amenewa,Chifukwa iye ndi amene anapanga china chilichonse,Ndipo Isiraeli ndi ndodo ya cholowa chake.+ Dzina lake ndi Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.+ 17  Iwe mkazi amene wazunguliridwa ndi adani,Sonkhanitsa katundu wako. 18  Chifukwa Yehova wanena kuti: “Pa nthawi ino ndikuthamangitsa* anthu okhala mʼdzikoli,+Ndipo ndidzachititsa kuti akumane ndi mavuto.” 19  Tsoka kwa ine chifukwa cha kuwonongedwa kwanga!*+ Bala langa ndi losachiritsika. Ndinanena kuti: “Ndithudi amenewa ndi matenda anga ndipo ndikufunika kuwapirira. 20  Tenti yanga yawonongedwa ndipo zingwe zanga zonse zomangira tentiyo aziduladula.+ Ana anga aamuna andisiya ndipo kulibenso.+ Palibe aliyense amene watsala woti atambasule tenti yanga kapena kudzutsa nsalu za tentiyo. 21  Abusa achita zinthu mopanda nzeru,+Ndipo sanafunse malangizo kwa Yehova.+ Nʼchifukwa chake sanachite zinthu mozindikira,Ndipo ziweto zawo zonse zabalalika.”+ 22  Tamvetserani, mdani akubwera! Kukumveka kugunda kwakukulu kuchokera kudziko lakumpoto,+Kumene kudzasandutsa mizinda ya Yuda kukhala mabwinja, malo obisalamo mimbulu.+ 23  Ine ndikudziwa bwino, inu Yehova, kuti munthu alibe ulamuliro wosankha yekha njira ya moyo wake. Munthu amene akuyenda alibe ulamuliro wowongolera mapazi ake.+ 24  Inu Yehova, ndilangizeni pondipatsa chiweruzo,Koma osati mutakwiya+ chifukwa mungandiwononge.+ 25  Tsanulirani mkwiyo wanu pa mitundu ya anthu amene akukunyalanyazani,+Komanso pa mafuko amene saitana pa dzina lanu. Chifukwa iwo awononga mbadwa zonse za Yakobo,+Amuwononga mpaka kufika potheratu,+Ndipo dziko lake alisandutsa bwinja.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “sompho wake.” Sompho ndi chida chimene mʼmadera ena amanena kuti kasemasema.
Vesi 11 poyamba linalembedwa mʼChiaramu.
Kapena kuti, “nthunzi.”
Kapena kuti, “mpweya.”
Kapena kuti, “Pa nthawi ino ndikutayira kutali.”
Kapena kuti, “chifukwa fupa langa lathyoka.”