Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Buku la Yeremiya

Machaputala

Mitu

  • 1

    • Yeremiya anasankhidwa kuti akhale mneneri (1-10)

    • Masomphenya a mtengo wa amondi (11, 12)

    • Masomphenya a mphika (13-16)

    • Yeremiya analimbikitsidwa kuti agwire ntchito yake (17-19)

  • 2

    • Isiraeli anasiya Yehova nʼkuyamba kulambira milungu ina (1-37)

      • Isiraeli ali ngati mtengo wa mpesa wachilendo (21)

      • Zovala zake zathimbirira ndi magazi (34)

  • 3

    • Isiraeli anapanduka kwambiri (1-5)

    • Isiraeli ndi Yuda anachita tchimo la chigololo (6-11)

    • Anawalimbikitsa kuti alape (12-25)

  • 4

    • Kulapa kumabweretsa madalitso (1-4)

    • Tsoka lidzachokera kumpoto (5-18)

    • Yeremiya anamva kupweteka mumtima chifukwa cha tsoka limene linkabwera (19-31)

  • 5

    • Anthu anakana malangizo a Yehova (1-13)

    • Adzawonongedwa koma sadzawawononga onse (14-19)

    • Yehova anaimba mlandu anthu (20-31)

  • 6

    • Nthawi yoti Yerusalemu azunguliridwe yayandikira (1-9)

    • Yehova anakwiyira Yerusalemu (10-21)

      • Akunena kuti, “Mtendere!” pamene kulibe mtendere (14)

    • Anaukiridwa mwankhanza ndi anthu akumpoto (22-26)

    • Yeremiya anasandutsidwa woyenga zitsulo (27-30)

  • 7

    • Kukhulupirira kachisi wa Yehova sikunawathandize (1-11)

    • Kachisi adzakhala ngati Silo (12-15)

    • Mulungu sasangalala ndi kulambira kwachinyengo (16-34)

      • Analambira “Mfumukazi Yakumwamba” (18)

      • Ankapereka nsembe ana ku Hinomu (31)

  • 8

    • Anthu anasankha njira imene anthu ambiri ankaitsatira (1-7)

    • Kodi anthu angakhale ndi nzeru popanda mawu a Yehova? (8-17)

    • Yeremiya analira chifukwa cha kuwonongedwa kwa Yuda (18-22)

      • “Kodi mu Giliyadi mulibe mafuta a basamu?” (22)

  • 9

    • Yeremiya anali ndi chisoni chachikulu (1-3a)

    • Yehova anaimba mlandu Yuda (3b-16)

    • Kulirira Yuda (17-22)

    • Adzitame chifukwa chodziwa Yehova (23-26)

  • 10

    • Milungu ya anthu a mitundu ina singafanane ndi Mulungu wamoyo (1-16)

    • Nthawi yoti awonongedwe komanso kutengedwa kupita kudziko lina yayandikira (17, 18)

    • Yeremiya anamva chisoni (19-22)

    • Pemphero la mneneri (23-25)

      • Munthu alibe ulamuliro wosankha yekha njira ya moyo wake (23)

  • 11

    • Yuda anaphwanya pangano limene anapanga ndi Mulungu (1-17)

      • Anali ndi milungu yochuluka mofanana ndi mizinda yawo (13)

    • Yeremiya anali ngati mwana wa nkhosa amene akupita kukaphedwa (18-20)

    • Yeremiya anatsutsidwa ndi anthu akwawo (21-23)

  • 12

    • Kudandaula kwa Yeremiya (1-4)

    • Zimene Yehova anayankha (5-17)

  • 13

    • Lamba wa nsalu amene anawonongeka (1-11)

    • Mitsuko ya vinyo idzaphwanyidwa (12-14)

    • Yuda amene sangathenso kusintha adzatengedwa kupita ku ukapolo (15-27)

      • “Kodi Mkusi angasinthe khungu lake?” (23)

  • 14

    • Chilala, njala ndi lupanga (1-12)

    • Aneneri abodza adzawonongedwa (13-18)

    • Yeremiya anavomereza kuti anthuwo anali ochimwa (19-22)

  • 15

    • Yehova sadzasintha chiweruzo chake (1-9)

    • Kudandaula kwa Yeremiya (10)

    • Zimene Yehova anayankha (11-14)

    • Pemphero la Yeremiya (15-18)

      • Ankasangalala ndi kudya mawu a Mulungu (16)

    • Yeremiya analimbikitsidwa ndi Yehova (19-21)

  • 16

    • Yeremiya anauzidwa kuti asakwatire, kulira kapena kusala kudya (1-9)

    • Anapatsidwa chilango kenako nʼkubwezeretsedwa mwakale (10-21)

  • 17

    • Tchimo la Yuda lalembedwa mochita kugoba (1-4)

    • Madalitso amene amabwera chifukwa chokhulupirira Yehova (5-8)

    • Mtima ndi wopusitsa (9-11)

    • Yehova, chiyembekezo cha Isiraeli (12, 13)

    • Pemphero la Yeremiya (14-18)

    • Sabata lizikhala lopatulika (19-27)

  • 18

    • Dongo mʼdzanja la wowumba (1-12)

    • Yehova adzafulatira Isiraeli (13-17)

    • Chiwembu chimene anakonzera Yeremiya komanso kuchonderera kwake (18-23)

  • 19

    • Yeremiya anauzidwa kuti akaswe botolo la dothi (1-15)

      • Kupereka ana nsembe kwa Baala (5)

  • 20

    • Pasuri anamenya Yeremiya (1-6)

    • Yeremiya sangasiye kulalikira (7-13)

      • Uthenga wa Mulungu unali ngati moto woyaka (9)

      • Yehova ali ngati msilikali woopsa (11)

    • Kudandaula kwa Yeremiya (14-18)

  • 21

    • Yehova anakana zimene Zedekiya anapempha (1-7)

    • Anthu ayenera kusankha pakati pa moyo ndi imfa (8-14)

  • 22

    • Uthenga wachiweruzo wokhudza mafumu oipa (1-30)

      • Uthenga wokhudza Salumu (10-12)

      • Uthenga wokhudza Yehoyakimu (13-23)

      • Uthenga wokhudza Koniya (24-30)

  • 23

    • Abusa abwino komanso oipa (1-4)

    • Tidzakhala otetezeka mu ulamuliro wa “mfumu yolungama” (5-8)

    • Aneneri abodza anadzudzulidwa (9-32)

    • “Katundu wolemera” wa Yehova (33-40)

  • 24

    • Nkhuyu zabwino komanso zoipa (1-10)

  • 25

    • Yehova anadzudzula mitundu ya anthu (1-38)

      • Mitundu ya anthu idzatumikira Ababulo kwa zaka 70 (11)

      • Kapu ya vinyo wa mkwiyo wa Mulungu (15)

      • Tsoka likufalikira kuchokera ku mtundu wina kupita ku mtundu wina (32)

      • Anthu amene adzaphedwe ndi Yehova (33)

  • 26

    • Yeremiya anaopsezedwa kuti aphedwa (1-15)

    • Yeremiya anapulumutsidwa (16-19)

      • Ananena zimene Mika ananena mu ulosi wake (18)

    • Mneneri Uliya (20-24)

  • 27

    • Goli la Babulo (1-11)

    • Zedekiya anauzidwa kuti azimvera mfumu ya Babulo (12-22)

  • 28

    • Yeremiya anatsutsana ndi mneneri wabodza Hananiya (1-17)

  • 29

    • Kalata imene Yeremiya analembera anthu amene anatengedwa ukapolo ku Babulo (1-23)

      • Aisiraeli adzabwerera kwawo pambuyo pa zaka 70 (10)

    • Uthenga wopita kwa Semaya (24-32)

  • 30

    • Malonjezo okhudza kubwezeretsedwa mwakale komanso kuchiritsidwa (1-24)

  • 31

    • Aisiraeli amene anatsala adzakhalanso mʼdziko lawo (1-30)

      • Rakele akulirira ana ake (15)

    • Pangano latsopano (31-40)

  • 32

    • Yeremiya anagula munda (1-15)

    • Pemphero la Yeremiya (16-25)

    • Zimene Yehova anayankha (26-44)

  • 33

    • Analonjezedwa kuti adzabwerera mwakale (1-13)

    • Tidzakhala otetezeka mu ulamuliro wa “mfumu yolungama” (14-16)

    • Pangano limene anachita ndi Davide komanso ansembe (17-26)

      • Pangano lokhudza masana ndi usiku (20)

  • 34

    • Uthenga wachiweruzo wopita kwa Zedekiya (1-7)

    • Anaphwanya pangano loti amasule akapolo (8-22)

  • 35

    • Arekabu anasonyeza chitsanzo chabwino pa nkhani yomvera (1-19)

  • 36

    • Yeremiya ankanena mawu oti alembedwe mumpukutu (1-7)

    • Baruki anawerenga mpukutu mokweza (8-19)

    • Yehoyakimu anawotcha mpukutu (20-26)

    • Uthengawo unalembedwanso mumpukutu watsopano (27-32)

  • 37

    • Akasidi anabwerera kwa kanthawi kochepa (1-10)

    • Yeremiya anaikidwa mʼndende (11-16)

    • Zedekiya anakumana ndi Yeremiya (17-21)

      • Yeremiya ankapatsidwa mkate (21)

  • 38

    • Yeremiya anaponyedwa mʼchitsime (1-6)

    • Ebedi-meleki anapulumutsa Yeremiya (7-13)

    • Yeremiya analimbikitsa Zedekiya kuti adzipereke mʼmanja mwa Ababulo (14-28)

  • 39

    • Kuwonongedwa kwa Yerusalemu (1-10)

      • Zedekiya anathawa koma anamugwira (4-7)

    • Yeremiya ankayenera kulonderedwa (11-14)

    • Ebedi-meleki anapulumutsidwa (15-18)

  • 40

    • Nebuzaradani anamasula Yeremiya (1-6)

    • Gedaliya anasankhidwa kuti akhale wolamulira dziko (7-12)

    • Chiwembu chimene anakonzera Gedaliya (13-16)

  • 41

    • Gedaliya anaphedwa ndi Isimaeli (1-10)

    • Yohanani anathamangitsa Isimaeli (11-18)

  • 42

    • Anthu anapempha Yeremiya kuti afunsire malangizo kwa Mulungu (1-6)

    • Yehova anawauza kuti: “Musapite ku Iguputo” (7-22)

  • 43

    • Anthu sanamvere ndipo anapita ku Iguputo (1-7)

    • Zimene Yehova anauza Yeremiya ku Iguputo (8-13)

  • 44

    • Ananeneratu za tsoka limene lidzagwere Ayuda ku Iguputo (1-14)

    • Anthu anakana kumvera zimene Mulungu anawachenjeza (15-30)

      • Ankalambira “Mfumukazi Yakumwamba” (17-19)

  • 45

    • Uthenga wa Yehova wopita kwa Baruki (1-5)

  • 46

    • Ulosi wokhudza Iguputo (1-26)

      • Iguputo adzagonjetsedwa ndi Nebukadinezara (13, 26)

    • Zimene Aisiraeli analonjezedwa (27, 28)

  • 47

    • Ulosi wokhudza Afilisiti (1-7)

  • 48

    • Ulosi wokhudza Mowabu (1-47)

  • 49

    • Ulosi wokhudza Aamoni (1-6)

    • Ulosi wokhudza Edomu (7-22)

      • Mtundu wa Edomu sudzakhalaponso (17, 18)

    • Ulosi wokhudza Damasiko (23-27)

    • Ulosi wokhudza Kedara ndi Hazori (28-33)

    • Ulosi wokhudza Elamu (34-39)

  • 50

    • Ulosi wokhudza Babulo (1-46)

      • Thawani mʼBabulo (8)

      • Aisiraeli adzawabwezera kwawo (17-19)

      • Madzi a ku Babulo adzaumitsidwa (38)

      • MʼBabulo simudzakhalanso anthu (39, 40)

  • 51

    • Ulosi wokhudza Babulo (1-64)

      • Babulo adzawonongedwa mwadzidzidzi ndi Amedi (8-12)

      • Buku linaponyedwa mumtsinje wa Firate (59-64)

  • 52

    • Zedekiya anagalukira mfumu ya Babulo (1-3)

    • Nebukadinezara anazungulira Yerusalemu (4-11)

    • Kuwonongedwa kwa mzinda komanso kachisi (12-23)

    • Anthu anatengedwa kupita ku ukapolo ku Babulo (24-30)

    • Yehoyakini anatulutsidwa mʼndende (31-34)