Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Buku la Miyambo

Machaputala

Mitu

  • 1

    • Cholinga cha miyambo (1-7)

    • Kuopsa kocheza ndi anthu amakhalidwe oipa (8-19)

    • Nzeru yeniyeni ikufuula mokweza mʼmabwalo (20-33)

  • 2

    • Ubwino wa nzeru (1-22)

      • Ufunefune nzeru ngati chuma chobisika (4)

      • Kuganiza bwino kumateteza (11)

      • Khalidwe lachiwerewere limabweretsa mavuto (16-19)

  • 3

    • Kukhala wanzeru komanso kudalira Yehova (1-12)

      • Kulemekeza Yehova pogwiritsa ntchito zinthu zamtengo wapatali (9)

    • Nzeru zimathandiza munthu kuti azisangalala (13-18)

    • Nzeru zimateteza (19-26)

    • Kuchitira ena zinthu zabwino (27-35)

      • Kuthandiza ena ngati tingathe (27)

  • 4

    • Malangizo anzeru a bambo (1-27)

      • Kuposa zonse, peza nzeru (7)

      • Kupewa njira zoipa (14, 15)

      • Njira ya wolungama imapitiriza kuwala (18)

      • “Uteteze mtima wako” (23)

  • 5

    • Chenjezo lokhudza akazi amakhalidwe oipa (1-14)

    • Sangalala ndi mkazi wako (15-23)

  • 6

    • Kukhala wosamala pa nkhani yolonjeza kubweza ngongole ya wina (1-5)

    • “Pita kwa nyerere waulesi iwe” (6-11)

    • Munthu wopanda nzeru komanso woipa (12-15)

    • Zinthu 7 zimene Yehova amadana nazo (16-19)

    • Samalani ndi mkazi wamakhalidwe oipa (20-35)

  • 7

    • Mverani malamulo a Mulungu kuti mukhale ndi moyo (1-5)

    • Mnyamata wosadziwa zinthu anakopedwa (6-27)

      • “Ngati ngʼombe yamphongo imene ikupita kukaphedwa” (22)

  • 8

    • Nzeru ikulankhula ngati munthu (1-36)

      • ‘Ine ndine woyamba kulengedwa ndi Mulungu’ (22)

      • ‘Ndinali pambali pake monga mmisiri waluso’  (30)

      • ‘Ndinkasangalala ndi ana a anthu’ (31)

  • 9

    • Nzeru yeniyeni ikuitana (1-12)

      • “Chifukwa ine ndidzachulukitsa masiku a moyo wako” (11)

    • Mkazi wopusa akuitana (13-18)

      • “Madzi akuba amatsekemera” (17)

  • MIYAMBI YA SOLOMO (10:1–24:34)

    • 10

      • Mwana wanzeru amasangalatsa bambo ake (1)

      • Wogwira ntchito mwakhama adzalemera (4)

      • Mawu akachuluka sipalephera kukhala zolakwika (19)

      • Madalitso a Yehova ndi amene amalemeretsa (22)

      • Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo (27)

    • 11

      • Anthu odzichepetsa ndi amene ali ndi nzeru (2)

      • Wampatuko amawononga anthu ena (9)

      • “Zinthu zimayenda bwino ngati pali alangizi ambiri” (14)

      • Munthu wopereka mowolowa manja zinthu zidzamuyendera bwino (25)

      • Munthu amene amadalira chuma chake adzakumana ndi mavuto (28)

    • 12

      • Amene amadana ndi kudzudzulidwa ndi wosaganiza bwino (1)

      • “Mawu a munthu amene amalankhula asanaganize amalasa ngati lupanga” (18)

      • Amene amalimbikitsa mtendere amasangalala (20)

      • Milomo yonama imamunyansa Yehova (22)

      • Nkhawa mumtima mwa munthu ndi imene imauweramitsa (25)

    • 13

      • Anthu amene amapempha malangizo amakhala ndi nzeru (10)

      • Chimene umayembekezera chikalephereka, mtima umadwala (12)

      • Nthumwi yokhulupirika imachiritsa (17)

      • Munthu woyenda ndi anthu anzeru adzakhala wanzeru (20)

      • Chilango chimasonyeza chikondi (24)

    • 14

      • Ngati munthu mtima ukumupweteka amadziwa yekha (10)

      • Njira imene imaoneka ngati yabwino ikhoza kubweretsa imfa (12)

      • Munthu amene sadziwa zambiri amakhulupirira mawu alionse (15)

      • Munthu wolemera amakhala ndi anzake ambiri (20)

      • Mtima wodekha umapangitsa kuti thupi likhale lathanzi (30)

    • 15

      • Kuyankha modekha kumabweza mkwiyo (1)

      • Maso a Yehova ali paliponse (3)

      • Pemphero la munthu wowongoka mtima limasangalatsa Mulungu (8)

      • Mapulani sakwaniritsidwa ngati anthu sakambirana (22)

      • Kuyamba waganiza usanayankhe (28)

    • 16

      • Yehova amafufuza zolinga zathu (2)

      • Zochita zako zonse uzisiye mʼmanja mwa Yehova (3)

      • Masikelo achilungamo ndi ochokera kwa Yehova (11)

      • Kunyada kumachititsa kuti munthu awonongeke (18)

      • Imvi ndi chisoti chachifumu cha ulemerero (31)

    • 17

      • Usabwezere zoipa mʼmalo mwa zabwino (13)

      • Mkangano usanabuke, chokapo (14)

      • Mnzako weniweni amakusonyeza chikondi nthawi zonse (17)

      • “Mtima wosangalala uli ngati mankhwala amene amachiritsa” (22)

      • Munthu wozindikira amapitiriza kukhala wodekha (27)

    • 18

      • Kudzipatula ndi kudzikonda komanso kupanda nzeru (1)

      • Dzina la Yehova ndi nsanja yolimba (10)

      • Chuma chili ngati chitetezo mʼmaganizo mwa munthu (11)

      • Ubwino womvetsera mbali zonse (17)

      • Mnzako amakhala nawe pafupi kuposa mʼbale wako (24)

    • 19

      • Kuzindikira kumachititsa kuti munthu abweze mkwiyo wake (11)

      • Mkazi wolongolola ali ngati denga lodontha (13)

      • Mkazi wanzeru amachokera kwa Yehova (14)

      • Langa mwana wako padakali chiyembekezo (18)

      • Ubwino womvetsera malangizo (20)

    • 20

      • Womwa vinyo wambiri amayamba kunyoza (1)

      • Waulesi salima nthawi yozizira (4)

      • Maganizo amumtima mwa munthu ali ngati madzi akuya (5)

      • Chenjezo pa nkhani yolumbira usanaganize bwino (25)

      • Ulemerero wa anyamata ndi mphamvu zawo (29)

    • 21

      • Yehova amatsogolera mtima wa mfumu (1)

      • Kuchita zinthu zachilungamo nʼkwabwino kuposa kupereka nsembe (3)

      • Khama limapindulitsa (5)

      • Amene samvetsera munthu wonyozeka nayenso sadzamvetseredwa (13)

      • Palibe nzeru zotsutsana ndi Yehova (30)

    • 22

      • Ndi bwino kusankha dzina labwino kusiyana ndi chuma chochuluka (1)

      • Ukaphunzitsa mwana zimamuyendera moyo wake wonse (6)

      • Munthu waulesi amanena kuti panja pali mkango (13)

      • Chilango chimachotsa uchitsiru (15)

      • Munthu waluso pa ntchito yake amatumikira mafumu (29)

    • 23

      • Muzichita zinthu mozindikira akakuitanirani chakudya (2)

      • Musamafunefune chuma (4)

      • Chuma chikhoza kuuluka nʼkupita kutali (5)

      • Usakhale mʼgulu la zidakwa (20)

      • Mowa umaluma ngati njoka (32)

    • 24

      • Usachitire nsanje anthu oipa (1)

      • Nzeru zimamanga nyumba ya munthu (3)

      • Munthu wolungama angagwe koma adzadzukanso (16)

      • Musamabwezere (29)

      • Kugona kumabweretsa umphawi (33, 34)

  • MIYAMBI INA YA SOLOMO IMENE ATUMIKI A MFUMU HEZEKIYA ANAKOPERA (25:1–29:27)

    • 25

      • Kusunga chinsinsi (9)

      • Mawu osankhidwa bwino (11)

      • Osamapitapita kunyumba kwa mnzako (17)

      • Kuunjika makala amoto pamutu pa mdani (21, 22)

      • Nkhani yabwino ili ngati madzi ozizira (25)

    • 26

      • Zimene anthu aulesi amachita (13-16)

      • Usamalowerere mkangano wa anthu ena (17)

      • Kupewa nthabwala zopusitsa ena (18, 19)

      • Ngati palibe nkhuni moto umazima (20, 21)

      • Mawu a munthu wonenera ena zoipa ali ngati chakudya chokoma (22)

    • 27

      • Kudzudzulidwa ndi mnzako nʼkothandiza (5, 6)

      • Mwana wanga sangalatsa mtima wanga (11)

      • Chitsulo chimanola chitsulo chinzake (17)

      • Uzidziwa bwino ziweto zako (23)

      • Chuma sichikhalitsa (24)

    • 28

      • Pemphero la munthu wosamvera ndi lonyansa (9)

      • Munthu woulula machimo ake amachitiridwa chifundo (13)

      • Amene amafuna kulemera mofulumira sadzalephera kukhala wolakwa (20)

      • Kudzudzula munthu kuli bwino kuposa kuyamikira mwachinyengo (23)

      • Munthu amene amapereka zinthu sadzasowa kanthu (27)

    • 29

      • Mwana womulekerera amachititsa manyazi (15)

      • Ngati anthu sakutsogoleredwa amachita zinthu motayirira (18)

      • Munthu wosachedwa kukwiya amayambitsa mkangano (22)

      • Munthu wodzichepetsa adzapeza ulemerero (23)

      • Kuopa anthu ndi msampha (25)

  • 30

    • MAWU A AGURI (1-33)

      • Musandipatse umphawi kapena chuma (8)

      • Zinthu zimene sizikhuta (15, 16)

      • Zinthu zimene njira zake sizidziwika (18, 19)

      • Mkazi wachigololo (20)

      • Nyama ndi zanzeru mwachibadwa (24)

  • 31

    • MAWU A MFUMU LEMUELI (1-31)

      • Ndani amene angapeze mkazi wamakhalidwe abwino? (10)

      • Amagwira ntchito mwakhama (17)

      • Kukoma mtima kuli palilime lake (26)

      • Ana ndi mwamuna wake amamutamanda (28)

      • Kuoneka bwino komanso kukongola sikuchedwa kutha (30)