Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NKHANI YA PACHIKUTO | KODI MUMATANI MUKAKUMANA NDI MAVUTO?

Kodi Mumatani Mukakumana ndi Mavuto?

Kodi Mumatani Mukakumana ndi Mavuto?

ANTHU ambiri amakonda kunena kuti, Pendapenda si kugwa. Choncho tisamataye mtima ngati penapake sizikutiyendera bwino. Masiku ano aliyense amakumana ndi mavuto. Koma chofunika n’kuvomereza mavutowo kenako n’kuona zimene tingakwanitse kuchita. N’zoona kuti mavuto ena akhoza kusintha koma kusintha kwenikweni kudzachitika m’dziko latsopano.

Baibulo limasonyeza kuti ikubwera nthawi pamene moyo wathu uzidzayenda bwinobwino. Tidzatha kuchita zonse zimene tikufuna popanda mavuto, kupanikizika kapena kukhumudwa. (Yesaya 65:21, 22) Baibulo limati umenewu udzakhala “moyo weniweniwo.”—1 Timoteyo 6:19.

“Iwo adzamanga nyumba n’kukhalamo. Adzabzala minda ya mpesa n’kudya zipatso zake. Sadzamanga wina n’kukhalamo. Sadzabzala wina n’kudya. Pakuti masiku a anthu anga adzakhala ngati masiku a mtengo, ndipo anthu anga osankhidwa mwapadera adzapindula mokwanira ndi ntchito ya manja awo.”—Yesaya 65:21, 22.