GALAMUKANI! July 2015 | Kodi Mumatani Mukakumana ndi Mavuto?

Kodi pa moyo wanu mwakumana ndi zinthu zimene simunkayembekezera? Magaziniyi ikufotokoza zimene zingakuthandizeni.

NKHANI YAPACHIKUTO

Kodi Mumatani Mukakumana ndi Mavuto?

Musataye mtima ngati mwakumana ndi mavuto osayembekezereka.

NKHANI YAPACHIKUTO

Vuto Limene Limakhalapo: Zinthu Zina Simungazisinthe

Onani zinthu 4 zimene zingakuthandizeni ngati mwakumana ndi vuto loti simungalisinthe.

NKHANI YAPACHIKUTO

Vuto Limene Limakhalapo: Kupanikizika

Mukamayesa kuchita zonse nokha mukhoza kulephera kuchita chilichonse. Kodi mungatani kuti musamapanikizike?

NKHANI YAPACHIKUTO

Vuto Limene Limakhalapo: Kukhala Wosasangalala

Kodi mungatani ngati mukuvutika chifukwa cha nkhawa, kukwiya kapena kukhumudwa? Onani zimene mungachite.

NKHANI YAPACHIKUTO

Kodi Mumatani Mukakumana ndi Mavuto?

N’zotheka kudziwa zochita mukakumana ndi mavuto.

ANTHU NDI MAYIKO

Dziko la Mongolia

Moyo wa anthu ambiri ku Mongolia ndi wongoyendayenda koma amalandira bwino alendo.

MFUNDO ZOTHANDIZA MABANJA

Kodi Mungatani Ngati Chibwenzi Chatha?

N’chiyani chingakuthandizeni ngati chibwenzi chanu chatha?

ZIMENE BAIBULO LIMANENA

Ntchito

Kodi mungasankhe bwanji ntchito?

Kodi Mukudziwa Zotani pa Nkhani ya Malungo?

Mukhoza kudziteteza ngati mumakhala kapena mukupita kudziko limene kuli malungo.

KODI ZINANGOCHITIKA ZOKHA?

Nsagwada za Ng’ona

Ng’ona ikaluma, mphamvu zake tingaziyerekezere ndi mphamvu za kuluma kwa mkango ndiyeno n’kuziwirikiza katatu. Koma nsagwada za ng’ona zikakhudzidwa ndi zinazake ng’onayo imamva mwamsanga kuposa mmene munthu amamvera chala chikakhudzidwa. Kodi izi zimatheka bwanji?

Zina zimene zili pawebusaiti

Kuba N’koipa

Kodi Mulungu amakuona bwanji kuba? Werengani Ekisodo 20:15. Onerani vidiyoyi kuti mudziwe zambiri limodzi ndi Kalebe.