Pitani ku nkhani yake

Kodi Mdyerekezi Angalamulire Zochita za Anthu?

Kodi Mdyerekezi Angalamulire Zochita za Anthu?

Yankho la m’Baibulo

 Zimene Mdyerekezi ndiponso ziwanda zimachita zimakhudza kwambiri zochita za anthu moti Baibulo limati: “Dziko lonse lili m’manja mwa woipayo.” (1 Yohane 5:19) Baibulo limatiuza njira zimene Mdyerekezi amagwiritsa ntchito pofuna kusocheretsa anthu.

  •   Chinyengo. Baibulo limalimbikitsa Akhristu kuti ‘azilimbana ndi zochita zachinyengo za Mdyerekezi.’ (Aefeso 6:11) Imodzi mwa njira zake zachinyengo ndi yakuti amapusitsa anthu kuti aziona ngati atumiki ake ndi atumiki a Mulungu.—2 Akorinto 11:13-15.

  •   Kukhulupirira mizimu. Mdyerekezi amasocheretsa anthu pogwiritsa ntchito anthu olankhula ndi mizimu, olosera za m’tsogolo ndiponso anthu ochita zamatsenga kapena okhulupirira nyenyezi. (Deuteronomo 18:10-12) Zinthu zinanso zimene zimachititsa kuti munthu akodwe mumsampha wa ziwanda n’kugwiritsa ntchito mankhwala ogwirizana ndi mizimu, kugonekedwa tulo m’matsenga ndiponso kusinkhasinkha kogwirizana ndi mizimu.—Luka 11:24-26.

  •   Chipembedzo chonyenga. Zipembedzo zimene zimaphunzitsa anthu zinthu zabodza zimachititsa kuti anthuwo asamamvere Mulungu. (1 Akorinto 10:20) Baibulo limanena kuti zinthu zabodza zimene chipembedzo chonyenga chimaphunzitsa ndi “ziphunzitso za ziwanda.”—1 Timoteyo 4:1.

  •   Kugwidwa ndi ziwanda. M’Baibulo muli nkhani zosonyeza kuti mizimu yoipa imalamulira anthu ena. Nthawi zina ziwandazo zinkachititsa khungu anthuwo kapena kuwachititsa kuti asamalankhule, ngakhalenso kuwavulaza kumene.—Mateyu 12:22; Maliko 5:2-5.

Zimene mungachite kuti Mdyerekezi asamakulamulireni

 Musachite mantha kuti mwina ziwanda zingayambe kukulamulirani chifukwa Baibulo limasonyeza kuti mungathe kukana zoti Mdyerekezi azikulamulirani.

  •   Muzitha kuzindikira ndi kudziwa bwino ziwembu za Mdyerekezi n’cholinga choti asakukoleni.—2 Akorinto 2:11.

  •   Muziphunzira mfundo za m’Baibulo n’kumazigwiritsa ntchito. Kuchita zimenezi kudzakuthandizani kuti musakodwe ndi misampha ya Mdyerekezi.—Aefeso 6:11-18.

  •   Mutaye kapena kuwotcha chinthu chilichonse chimene chikugwirizana ndi ziwanda. (Machitidwe 19:19) Zinthu zimenezi zingakhale nyimbo, mabuku, magazini, zithunzi ndiponso mavidiyo amene amalimbikitsa zamizimu.