Kodi Baibulo Ndi Buku la Azungu?
Yankho la m’Baibulo
Baibulo silinalembedwe ndi azungu. Anthu onse amene Mulungu anawagwiritsira ntchito polemba Baibulo anali a ku Asia. Ndipotu, Baibulo silisonyeza kuti mtundu wina wa anthu ndi wapamwamba kuposa mtundu wina. Baibulo limanena kuti: “Mulungu alibe tsankho. Iye amalandira munthu wochokera mu mtundu uliwonse, amene amamuopa ndi kuchita chilungamo.”—Machitidwe 10:34, 35.