Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo

Buku ino idzakufotokozelani nkhani zolekana-lekana, kuyambila pa nkhani ya m’baibo ya cilengedwe, kubadwa kwa Yesu na utumiki wake, mpaka za Ufumu umene udzabwela.

Kalata Yocokela ku Bungwe Lolamulila

Kodi tingaiseŵenzetse bwanji buku ino?

PHUNZILO 1

Mulungu Anapanga Kumwamba na Dziko Lapansi

Baibo imati Mulungu anapanga kumwamba na dziko lapansi. N’cifukwa ciani Mulungu analenga mngelo mmodzi coyamba akalibe kulenga cina ciliconse kapena wina aliyense?

PHUNZILO 2

Mulungu Anapanga Mwamuna na Mkazi Woyamba

Mulungu anapanga mwamuna na mkazi woyamba na kuŵaika m’munda wa Edeni. Anali kufuna kuti iwo akhale ndi ana na kupanga dziko lonse kukhala paradaiso.

PHUNZILO 3

Adamu na Hava Sanamvele Mulungu

N’ciani cinali capadela ndi mtengo umodzi wa m’munda wa Edeni? N’cifukwa ciani Hava anadya cipatso ca mu mtengowo?

PHUNZILO 4

Kukwiya Mpaka Kupha Munthu

Mulungu analandila nsembe ya Abele osati ya Kaini. Kaini atadziŵa, akwiya kwambili na kucita cinthu coipa maningi.

PHUNZILO 5

Cingalawa ca Nowa

Angelo oipa atakwatila akazi pa dziko, anakhala na viŵana vimphona vankhanza ngako. Ciwawa cinali paliponse. Koma Nowa sanali ngati anthu amenewo—iye anali kukonda Mulungu na kumumvela.

PHUNZILO 6

Anthu 8 Anapulumuka na Kulowa m’Dziko Latsopano

Cimvula cinagwa kwa masiku 40 usana na usiku. Nowa na banja lake anakhala m’cingalawa kuposa caka cimodzi. Potsilizila, anatuluka m’cingalawa.

PHUNZILO 7

Nsanja ya Babele

Anthu anafuna kumanga mzinda na nsanja yaitali yokafika kumwamba kweni-kweni. N’cifukwa ciani Mulungu mwadzidzidzi anawacititsa kuyamba kukamba vitundu vosiyana-siyana?

PHUNZILO 8

Abulahamu na Sara Anamvela Mulungu

N’cifukwa ciani Abulahamu na Sara anasiya umoyo wabwino n’kupita ku dziko la Kanani kukakhala alendo?

PHUNZILO 9

Mpaka anakhala na mwana wake!

Kodi Mulungu anakwanilitsa bwanji lonjezo lake kwa Abulahamu? Ni mwana uti wa Abulahamu amene kupitila mwa iye, lonjezo limeneli linakwanilitsidwa—Isaki kapena Isimaeli?

PHUNZILO 10

Kumbukilani Mkazi wa Loti

Mulungu anagwetsa moto na sulufule pa Sodomu na Gomora. N’cifukwa ciani mizinda imeneyi inawonongedwa? N’cifukwa ciani tiyenela kukumbukila mkazi wa Loti?

PHUNZILO 11

Cikhulupililo Ciyesedwa

Mulungu anauza Abulahamu kuti: ‘Tenga mwana wako mmodzi yekhayo ndipo ukamupeleke nsembe pa phili ku Moriya.’ Kodi Abulahamu akanacita ciani na nkhani yoyesa cikhulupililo imeneyi?

PHUNZILO 12

Yakobo Analandila Coloŵa

Isaki na Rabeka pamodzi na ana awo aŵili amphundu. Maina awo anali Esau na Yakobo. Popeza Esau ndiye anali woyamba kubadwa, anali kudzalandila coloŵa capadela. N’cifukwa ciani anasinthanitsa coloŵaco na mbale imodzi ya cakudya?

PHUNZILO 13

Yakobo na Esau Akhalanso pa Mtendele

N’cifukwa ciani Yakobo anadalitsidwa na mngelo? Nanga anacita ciani kuti akhalenso pa mtendele na Esau?

PHUNZILO 14

Kapolo Amene Anamvela Mulungu

Yosefe anali kucita zabwino, koma anakumanabe na mavuto aakulu. Cifukwa ciani?

PHUNZILO 15

Yehova Sanamuiŵalepo Yosefe

Ngakhale kuti Yosefe anali kutali na banja lake, Mulungu anaonetsa kuti anali naye.

PHUNZILO 16

Kodi Yobu Anali Ndani?

Anamvela Yehova ngakhale kuti zinali zovuta.

PHUNZILO 17

Mose Anasankha Kulambila Yehova

Ali mwana, Mose anapulumuka cifukwa amayi ake anacita zinthu mwanzelu.

PHUNZILO 18

Citsamba Coyaka Moto

N’cifukwa ciani citsamba sicinali kupsa na moto?

PHUNZILO 19

Milili Itatu Yoyambilila

Farao anabweletsa mavuto pa anthu ake. Cifukwa conyada, anakana kucita cinthu cosavuta.

PHUNZILO 20

Milili 6 Yokonkhapo

Kodi milili imeneyi inasiyana bwanji na itatu yoyambilila?

PHUNZILO 21

Mlili wa Namba 10

Mlili umenewu unali woopsa kwambili cakuti Farao wonyadayo anagonja.

PHUNZILO 22

Cozizwitsa pa Nyanja Yofiila

Farao anapulumuka milili 10. Koma kodi anapulumuka cozizwitsa ici ca Mulungu?

PHUNZILO 23

Lonjezo kwa Yehova

Aisiraeli anacita pangano lapadela kwa Mulungu atamanga misasa pafupi na Phili la Sinai.

PHUNZILO 24

Anaphwanya Lonjezo Lawo

Pamene Mose anali kulandila Mamulo 10, Aisiraeli anacita chimo lalikulu.

PHUNZILO 25

Cihema Colambililako

M’cihema capadela cimeneci munali likasa la cipangano.

PHUNZILO 26

Azondi 12

Yoswa na Kalebe anali osiyana ndi amuna ena 10 amene anazonda dziko la Kanani.

PHUNZILO 27

Anapandukila Yehova

Kora, Datani, Abiramu, na anthu ena 250 analephela kuzindikila mfundo yofunika yokhudza Yehova.

PHUNZILO 28

Bulu wa Balamu Akamba

Bulu anaona wina wake amene Balamu sanamuone.

PHUNZILO 29

Yehova Asankha Yoswa

Mulungu anapatsa Yoswa malangizo amene na ise angatithandize masiku ano.

PHUNZILO 30

Rahabi Abisa Azondi

Mpanda wa Yeriko unagwa, koma nyumba ya Rahabi siinagwe olo kuti inali yolumikizika ku mpandawo.

PHUNZILO 31

Yoswa na Agibeoni

Yoswa anapemphela kwa Mulungu kuti: “Dzuŵa iwe, ima!” Kodi Mulungu anayankha?

PHUNZILO 32

Mtsogoleli Watsopano na Azimayi Aŵili Olimba Mtima

Pamene Yoswa anamwalila, Aisiraeli anayamba kulambila mafano. Umoyo unali wovuta, koma anathandizidwa kupitila mwa Oweruza Baraki, mneneli wamkazi Debora, na Yaeli amene anaseŵenzetsa cimphompho ca tenthi!

PHUNZILO 33

Rute na Naomi

Akazi aŵili amene amuna awo anafa anabwelela ku isiraeli. Mmodzi wa iwo, Rute, anapita kukakunkha m’minda, kumene Boazi anamuona.

PHUNZILO 34

Gidiyoni Agonjetsa Amidiyani

Amidiyani atapangitsa umoyo wa Aisiraeli kukhala wovuta, Aisiraeli anacondelela Yehova kuti awathandize. Kodi gulu locepa la asilikali a Gidiyoni linacita ciani kuti ligonjetse gulu la adani lokhala na asilikali 135,000?

PHUNZILO 35

Hana Apemphela Kuti Akhale na Mwana

Elikana pamodzi na Hana, Penina na banja lake anapita kukalambila ku cihema ku Silo. Kumeneko Hana anapemphela kuti akhale na mwana. Caka cotsatila iye anabeleka Samueli!

PHUNZILO 36

Lonjezo la Yefita

Kodi Yefita anapanga lonjezo lotani, ndipo cifukwa ciani? Nanga mwana wake anacita ciani atamvela za lonjezo la Atate ake?

PHUNZILO 37

Yehova Akamba na Samueli

Eli Mkulu wa Ansembe, anali ndi ana aamuna aŵili otumikila monga ansembe pa cihema. Iwo sanali kumvela malamulo a Yehova. Koma wacicepele Samueli anali womvela, ndipo Yehova anakamba naye.

PHUNZILO 38

Yehova Anapatsa Mphamvu Samsoni

Mulungu anapatsa mphamvu Samsoni kuti agonjetse Afilisiti, koma pamene Samsoni anapanga cosankha colakwika, Afilisiti anamugwila.

PHUNZILO 39

Mfumu Yoyamba ya Aisiraeli

Mulungu anapatsa Aisiraeli oweluza kuti aziŵatsogolela, koma iwo anafuna mfumu. Samueli anadzoza Sauli kukhala mfumu yoyamba, koma pambuyo pake Yehova anam’kana Sauli. Cifukwa ciani?

PHUNZILO 40

Davide na Goliyati

Yehova asankha Davide kukhala mfumu yotsatila ya Aisiraeli, ndipo Davide aonetsa cifukwa cake anasankhidwa.

PHUNZILO 41

Davide na Sauli

N’cifukwa ciani mmodzi wa anthu awa amazonda mnzake? Nanga mnzakeyo acita zinthu motani?

PHUNZILO 42

Yonatani, Munthu Wolimba Mtima Komanso Wokhulupilika

Mwana wa mfumu akhala bwenzi lapamtima la Davide.

PHUNZILO 43

Chimo ya Mfumu Davide

Kusankha molakwika kumabweletsa mavuto ambili.

PHUNZILO 44

Kacisi wa Yehova

Mulungu ayankha pempho ya Mfumu Solomo ndipo am’dalitsa m’njila zambili.

PHUNZILO 45

Ufumu Ugaŵika

Aisiraeli ambili asiya kulambila Yehova.

PHUNZILO 46

Mulungu Woona Adziŵika pa Phili la Karimeli

Kodi Mulungu woona n’ndani? Yehova kapena Baala?

PHUNZILO 47

Yehova Alimbikitsa Eliya

Kodi uganiza kuti na iwe angakulimbikitse?

PHUNZILO 48

Mwana wa Mkazi Wamasiye Aukitsidwa

Zozizwitsa ziŵili m’nyumba imodzi!

PHUNZILO 49

Mfumukazi Yoipa Inalangiwa

Yezebeli akonza zakupha Mwisiraeli wina dzina lake Naboti, n’colinga cofuna kutenga munda wake wampesa! Kuipa komanso kupanda cilungamo kwake, Yehova Mulungu wakuona.

PHUNZILO 50

Yehova Anateteza Yehosafati

Yehosafati mfumu yabwino ipemphela kwa Mulungu pamene Ayuda awopsezedwa na mitundu yodana nawo.

PHUNZILO 51

Kamtsikana Kathandiza Mkulu wa Asilikali

Kamtsikana kaciisiraeli kauza adona ake za mphamvu zazikulu za Yehova za kucilitsa mozizwitsa.

PHUNZILO 52

Asilikali a Yehova Amoto

Mmene mtumiki wa Elisa anaonela kuti ‘tili na ambili kumbali yathu kuposa amene ali kumbali yawo.’

PHUNZILO 53

Yehoyada Anali Wolimba Mtima

Mosasamala kanthu za mfumukazi yoipa, wansembe wokhulupilika aonetsa kulimba mtima.

PHUNZILO 54

Yehova Anamulezela Mtima Yona

Kodi cinacitika n’ciani kuti mmodzi wa aneneli a Mulungu amezedwe na cinsomba cacikulu? Nanga anacokamo bwanji? Kodi Yehova anam’phunzitsa ciani?

PHUNZILO 55

Mngelo wa Yehova Ateteza Hezekiya

Adani a Ayuda akuti Yehova sadzateteza anthu ake, koma zimenezi si zoona!

PHUNZILO 56

Yosiya Anali Kukonda Cilamulo ca Mulungu

Yosiya akhala mfumu ali na zaka 8 cabe, ndipo athandiza anthu kuyamba kulambila Yehova.

PHUNZILO 57

Yehova Atumiza Yeremiya Kuti Akalalikile

Zimene mneneli wacicepele uyu anakamba, zinawakwiitsa kwambili akulu-akulu a Yuda.

PHUNZILO 58

Yerusalemu Awonongedwa

Ayuda apitiliza kulambila milungu yabodza, ndiyeno Yehova awasiya.

PHUNZILO 59

Anyamata Anayi Amene Anamvela Yehova

Anyamata aciyuda sanaleke kukhulupilila Yehova, ngakhale ali ku nyumba kwa mfumu nebukadinezara ku Babulo.

PHUNZILO 60

Ufumu Umene Udzalamulila Kwamuyaya

Danieli amasulila tanthauzo la maloto odabwitsa a Nebukadinezara.

PHUNZILO 61

Anakana Kugwadila Fano

Sadirake, Mesake, na Abedinego akana kulambila fano lagolide la mfumu ya Babulo.

PHUNZIIO 62

Ufumu Umene Uli Monga Mtengo Waukulu

Maloto a Nebukadinezara alosela za tsogolo la iye mwini.

PHUNZILO 63

Dzanja Lilemba pa Cipupa

Kodi mawu osadziŵika anaonekela pa nthawi iti? Nanga atanthauza ciani?

PHUNZILO 64

Danieli Aponyedwa m’Dzenje la Mikango

Pemphelani kwa Yehova tsiku lililonse, monga mmene Danieli anali kucitila!

PHUNZILO 65

Mfumukazi Esitere Apulumutsa Anthu a Mtundu Wake

Ngakhale kuti anali ku dziko la eni, zinthu zinasintha kucoka pa mwana wamasiye n’kukhala mfumukazi.

PHUNZILO 66

Ezara Aphunzitsa Cilamulo ca Mulungu

Aisiraeli atamvetsela kwa Ezara, iwo anapanga lonjezo lapadela kwa Mulungu.

PHUNZILO 67

Mpanda wa Yerusalemu Umangidwanso

Nehemiya anadziŵa kuti adani ake afuna kuukila. Koma n’cifukwa ciani sanacite mantha?

PHUNZILO 68

Elizabeti Akhala na Mwana

N’cifukwa ciani mwamuna wa Elizabeti anauzidwa kuti adzaleka kukamba mpaka mwana akabadwe?

PHUNZILO 69

Gabirieli Aonekela kwa Mariya

Amuuza uthenga umene udzasintha moyo wake wonse

PHUNZILO 70

Angelo Analengeza za Kubadwa kwa Yesu

Abusa amene anamvela cilengezo ca kubadwa kwa Yesu anacitapo kanthu mwamsanga.

PHUNZILO 71

Yehova Anam’teteza Yesu

Mfumu yoipa inafuna kupha Yesu.

PHUNZILO 72

Pamene Yesu Anali Wacicepele

Kodi n’ciani cinadabwitsa aphunzitsi pakacisi ponena za Yesu?

PHUNZILO 73

Yohane Anakonza Njila

Pamene Yohane wakula akhala mneneli. Iye aphunzitsa anthu kuti Mesiya adzabwela. Kodi anthu aulandila bwanji uthenga wake?

PHUNZILO 74

Pamene Yesu Anakhala Mesiya

Kodi Yohane atanthauza ciani pokamba kuti Yesu ni Mwanawankhosa wa Mulungu?

PHUNZILO 75

Mdyelekezi Ayesa Yesu

Katatu konse Mdyelekezi ayesa Yesu. Kodi ni mayeselo atatu ati amene ayesedwa nawo? Nanga Yesu ayankha bwanji?

PHUNZILO 76

Yesu Ayeletsa Kacisi

N’cifukwa ciani Yesu akuthamangitsa nyama m’kacisi, na kugubuduza mathebulo a osintha ndalama?

PHUNZILO 77

Mzimayi Akumana na Yesu pa Citsime

Mzimayi wacisamariya adabwa kuona kuti Yesu akukamba naye. Cifukwa? Kodi Yesu amuuza ciani mzimayiyo cimene sauzepo munthu aliyense?

PHUNZILO 78

Yesu Analalikila Uthenga wa Ufumu

Yesu auza ophunzila ake kukhala “asodzi a anthu.” M’kupita kwa nthawi, Yesu aphunzitsa anthu 70 nchito yolalikila uthenga wabwino.

PHUNZILO 79

Yesu Acita Zozizwitsa Zambili

Kulikonse kumene wayenda, anthu odwala abwela kwa iye kuti awacilitse, ndipo awacilitsadi. Iye aukitsa ngakhale kamtsikana kamene kamwalila.

PHUNZILO 80

Yesu Asankha Atumwi 12

Kodi Yesu wasankha atumwi 12 kuti agwile nchito yanji? Kodi ungakumbukile maina awo?

PHUNZILO 81

Ulaliki wa pa Phili

Yesu aphunzitsa mfundo zofunika kwambili ku khamu la anthu limene lasonkhana.

PHUNZILO 82

Yesu Anaphunzitsa Otsatila Ake Kupemphela

Kodi ni zinthu zotani zimene auza otsatila ake kupitiliza kupempha?

PHUNZILO 83

Yesu Anadyetsa Khamu la Anthu

Kodi cozizwitsa ici citiphunzitsa ciani za Yesu na Yehova?

PHUNZILO 84

Yesu Anayenda pa Madzi

Kodi uganiza kuti atumwi amvela bwanji pamene akuona cozizwitsa cimeneci?

PHUNZILO 85

Yesu Acilitsa pa Sabata

N’cifukwa ciani ena sanakondwele na zimene Yesu acita?

PHUNZILO 86

Yesu Aukitsa Lazaro

Pamene Yesu aona Mariya akulila, nayenso ayamba kulila. Koma mwamsanga cisoni cawo cisintha kukhala cimwemwe.

PHUNZILO 87

Mgonelo wa Ambuye

Yesu apeleka malangizo ofunika kwa atumwi ake.

PHUNZILO 88

Am’gwila Yesu

Yudasi Isikariyoti atsogolela cigulu ca anthu cokhala na malupanga na zibonga kuti akagwile Yesu.

PHUNZILO 89

Petulo Akana Yesu

Kodi n’ciani cicitika m’bwalo la nyumba ya Kayafa? Nanga n’ciani cicitikila Yesu m’nyumba ya Kayafa?

PHUNZILO 90

Yesu Aphedwa ku Gologota

N’cifukwa ciani Pilato walamula kuti Yesu aphedwe?

PHUNZILO 91

Yesu Aukitsidwa

Kodi ni zinthu zodabwitsa ziti zimene zicitika pambuyo pakuti Yesu waphedwa?

PHUNZILO 92

Yesu Aonekela kwa Ophunzila Ake Asodzi

Kodi Yesu acita ciani kuti ophunzila ake amumvetsele?

PHUNZILO 93

Yesu Abwelela Kumwamba

Asanabwelele, apatsa ophunzila ake malangizo ena ofunika kwambili.

PHUNZILO 94

Ophunzila a Yesu Alandila Mzimu Woyela

Kodi mzimu woyela uŵapangitsa kucita zozizwitsa zotani?

PHUNZILO 95

Palibe Akanawaletsa Kulalikila

Atsogoleli acipembedzo amene anapha Yesu, lomba akuopseza atumwi kuti aleke kulalikila. Koma iwo alephela.

PHUNZILO 96

Yesu Asankha Saulo

Saulo ni mdani wankhanza wa Akhristu, koma zinthu zatsala pang’ono kusintha.

PHUNZILO 97

Koneliyo Alandila Mzimu Woyela

N’cifukwa ciani Mulungu watumiza Petulo kwa munthu uyu amene si Myuda?

PHUNZILO 98

Cikhristu Cifalikila Kumadela Akutali

Mtumwi Paulo pamodzi na amishonale anzake ayamba nchito yolalikila kumadela akutali.

PHUNZILO 99

Woyang’anila Ndende Aphunzila Coonadi

N’cifukwa ciani Paulo na Sila aponyedwa m’ndende? Nanga woyang’anila ndende aphunzila bwanji coonadi

PHUNZILO 100

Paulo na Timoteyo

Kwa zaka zambili, amuna aŵiliwa aseŵenzela pamodzi monga mabwenzi komanso atumiki a Mulungu.

PHUNZILO 101

Paulo Atumizidwa ku Roma

Pa ulendowu, akumana na zovuta zambili. Koma palibe vuto lililonse lingapangitse mtumwiyu kubwelela kumbuyo.

PHUNZILO 102

Masomphenya a Yohane

Yesu amuonetsa masomphenya osiyana-siyana a zakutsogolo.

PHUNZILO 103

“Ufumu Wanu Ubwele”

Masomphenya amene Yohane aona, akuonetsa mmene Ufumu wa Mulungu udzasinthila umoyo pa dziko lapansi.