Pitani ku nkhani yake

M’bale Aleksandr Nikolayev ndi mkazi wake Yevgeniya

30 DECEMBER, 2021
RUSSIA

M’bale Nikolayev Anapeza Mtendere Chifukwa Chokhulupirira Yehova

M’bale Nikolayev Anapeza Mtendere Chifukwa Chokhulupirira Yehova

Nthawi Komanso Zimene Zinachitika

  1. 23 December, 2021

    Khoti la m’boma la Abinskiy m’chigawo cha Krasnodar linapeza kuti m’bale Aleksandr Nikolayev ndi wolakwa ndipo anamugamula kuti akakhale m’ndende kwa zaka ziwiri ndi miyezi 6

  2. 30 September, 2021

    Anakaikidwa m’ndende poyembekezera chigamulo

  3. 4 August, 2021

    Mlandu wawo unayamba kuzengedwa

  4. 26 May, 2021

    Anaimbidwa mlandu chifukwa choti anamupeza akukambirana mfundo za m’Baibulo ndi achibale ake komanso anzake. Apolisi anaona kuti umenewu unali “mlandu wophwanya malamulo oyendetsera dzikolo komanso kusokoneza chitetezo”

  5. 7 April, 2021

    6 koloko m’mawa apolisi a FSB komanso apolisi ena oletsa zachiwawa anabwera kudzafufuza zinthu m’nyumba ya a Nikolayev. Kenako anapita nawo ku polisi komwe anakawapanikiza ndi mafunso ndipo pambuyo pake anawalola kubwerera kunyumba

  6. 31 March, 2021

    Anawatsegulira mlandu wophwanya malamulo

Zokhudza m’baleyu

Tili ndi chikhulupiriro kuti m’bale Nikolayev komanso abale ndi alongo ena a ku Russia ndi ku Crimea, adzadalitsidwa chifukwa chopitiriza kukhulupirira ndi kudalira Yehova.—Yeremiya 17:7.